Masalmo 100:1 Fuulirani kwa Yehova, maiko inu nonse. 100: 2 Tumikirani Yehova mokondwera: Idzani pamaso pake ndi kuyimba. 100:3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu: Iye ndi amene anatilenga, osati ife tokha; ndife anthu ake, ndi nkhosa za pabusa pake. 100:4 Lowani m'zipata zake ndi chiyamiko, ndi m'mabwalo ake ndi matamando. muyamike, nimulemekeze dzina lake. 100:5 Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake nchosatha; ndipo choonadi chake chikhalitsa ku mibadwo yonse.