Agalatiya 6 Heb 6:1 Abale, ngati munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu. bweza wotere mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, kuti kapena iwenso uyesedwe. Joh 6:2 Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mukwaniritse chilamulo cha Khristu. Heb 6:3 Pakuti ngati munthu adziyesa kanthu pokhala ali chabe, ali chabe adzinyenga yekha. Mar 6:4 Koma yense ayesere ntchito yake ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kukondwera mwa Iye yekha, si mwa wina. Joh 6:5 Pakuti munthu aliyense adzasenza katundu wake wa iye yekha. Joh 6:6 Iye wophunzitsidwa mawu agawane ndi wophunzitsa zabwino zonse. Joh 6:7 Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, ndicho iyenso adzatuta. Rev 6:8 Pakuti wakufesera kwa thupi lake, chochokera m'thupi adzatuta chibvundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha. 6:9 Ndipo tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta; ngati sitikomoka. 6:10 Chifukwa chake, monga tili ndi mwayi, tichitire anthu onse chokoma. makamaka kwa iwo a pabanja la chikhulupiriro. Joh 6:11 Muwona kukula kwake kalata ndakulemberani ndi dzanja langa la ine ndekha. Heb 6:12 Onse amene afuna kuonekera wokoma m'thupi, iwowa akukakamizani inu kudulidwa; kokha kuti angazunzike chifukwa cha iwo mtanda wa Khristu. Joh 6:13 Pakuti angakhale iwo wodulidwa sasunga chilamulo; koma kufuna kuti akudulidweni, kuti akadzitamandire m’thupi lanu. Heb 6:14 Koma kusandidzitamandira ine, koma mtanda wa Ambuye wathu Yesu Khristu Khristu, mwa amene dziko lapansi linapachikidwa kwa ine, ndi ine kwa dziko lapansi. Joh 6:15 Pakuti mwa Khristu Yesu mdulidwe ulibe mphamvu, kapena palibe kanthu wosadulidwa, koma wolengedwa watsopano. 6:16 Ndipo onse amene akuyenda monga mwa lamulo ili, mtendere ndi chifundo zikhale pa iwo. ndi pa Israyeli wa Mulungu. Joh 6:17 Kuyambira tsopano palibe munthu andibvute ine; pakuti ndiri nawo m'thupi langa zipsera wa Ambuye Yesu. Heb 6:18 Abale, chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Amene.