3 Yohane Heb 1:1 Mkulu, kwa Gayo wokondedwa, amene ndikondana naye m'chowonadi. Heb 1:2 Wokondedwa, ndikhumba pa zinthu zonse kuti ulemere, nukhalemo thanzi, monganso moyo wako upindula. Act 1:3 Pakuti ndidakondwera kwakukulu pamene adadza abale nachitira umboni za iwo chowonadi chiri mwa iwe, monga uyenda m'chowonadi. Heb 1:4 Ndilibe chimwemwe choposa kumva kuti ana anga akuyenda m'chowonadi. 1:5 Wokondedwa, uchita mokhulupirika chiri chonse uwachitira abale; ndi kwa alendo; Joh 1:6 Amene adachitira umboni za chikondi chako pamaso pa Mpingo; muwatsogolere monga mwa Mulungu, udzachita bwino; Mar 1:7 Pakuti chifukwa cha dzina lake adatuluka, osatenga kanthu kwa Iye Amitundu. Heb 1:8 Chifukwa chake tiyenera kulandira otere, kuti tikhale wothandizana nawo chowonadi. Php 1:9 Ndinalembera Mpingo; koma Diyotrefe, wokonda kukhala nawo ukulu wa iwo, sutilandira ife. Joh 1:10 Chifukwa chake, ndikadza, ndidzakumbukira ntchito zake zimene azichita, ndi kuyankhula kwake pa ife ndi mau oipa; Iye mwini alandira abale, nawaletsa iwo amene afuna; amawatulutsa iwo mu mpingo. Heb 1:11 Wokondedwa, usatsate choyipa, koma chabwino. Iye uyo achita zabwino achokera kwa Mulungu: koma wochita zoipa sanawona Mulungu. Joh 1:12 Demetriyo amchitira umboni wabwino anthu onse, ndi chowonadi chokha; ifenso tichitira umboni; ndipo mudziwa kuti umboni wathu uli woona. Joh 1:13 Ndidali nazo zambiri zolembera, koma sindifuna kuzilembera ndi inki ndi cholembera inu: Joh 1:14 Koma ndiyembekeza kuti ndidzakuwona iwe posachedwa, ndipo tidzayankhulana maso ndi maso. Mtendere ukhale ndi inu. Anzathu akupatsani moni. Moni kwa anzanuwo mwa mayina.